-
Salimo 72:1Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
72 Inu Mulungu, thandizani mfumu kuti iziweruza mogwirizana ndi zigamulo zanu,
Ndipo dziwitsani mwana wa mfumu za chilungamo chanu.+
-
-
Yesaya 9:7Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
7 Ulamuliro* wake udzafika kutali
Ndipo mtendere sudzatha,+
Pampando wachifumu wa Davide+ ndiponso mu ufumu wake
Kuti iye achititse ufumuwo kukhazikika+ ndiponso kukhala wolimba
Pogwiritsa ntchito chilungamo+ ndiponso mtima wowongoka,+
Kuyambira panopa mpaka kalekale.
Yehova wa magulu ankhondo akumwamba adzachita zimenezi modzipereka kwambiri.
-