Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • 2 Mafumu 19:14-19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 14 Hezekiya anatenga makalatawo mʼmanja mwa anthuwo nʼkuwawerenga. Kenako iye anapita nawo kunyumba ya Yehova nʼkuwatambasula pamaso pa Yehova.+ 15 Ndiyeno Hezekiya anayamba kupemphera+ kwa Yehova kuti: “Inu Yehova Mulungu wa Isiraeli wokhala pamwamba* pa akerubi,+ inu nokha ndinu Mulungu woona wa maufumu onse apadziko lapansi.+ Inuyo munapanga kumwamba ndi dziko lapansi. 16 Tcherani khutu lanu, inu Yehova, mumve.+ Tsegulani maso anu,+ inu Yehova, muone. Imvani mawu amene Senakeribu watumiza onyoza Mulungu wamoyo. 17 Nʼzoonadi Yehova, kuti mafumu a Asuri awononga mayiko ndi anthu a mʼmayikowo.+ 18 Aponya milungu yawo pamoto, chifukwa sinali milungu,+ koma ntchito ya manja a anthu,+ mitengo ndi miyala. Nʼchifukwa chake anatha kuiwononga. 19 Tsopano inu Yehova Mulungu wathu, chonde tipulumutseni mʼmanja mwake, kuti maufumu onse apadziko lapansi adziwe kuti inu nokha Yehova, ndinu Mulungu.”+

Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • tumizirani
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • zachinsinsi
  • JW.ORG
  • Lowani
tumizirani