-
Yeremiya 31:35-37Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
35 Yehova amene amapereka dzuwa kuti liziwala masana,
Amene amaika malamulo oti mwezi ndi nyenyezi ziziwala usiku,
Amene amavundula nyanja
Kuti mafunde ake achite phokoso,
Amene dzina lake ndi Yehova wa magulu ankhondo akumwamba, wanena kuti:+
36 “‘Ngati malamulo amenewa angalephere kugwira ntchito yake,
Ndiye kutinso mbadwa za Isiraeli zingasiye kukhala mtundu, umene umakhala pamaso panga nthawi zonse,’ akutero Yehova.”+
37 Yehova wanena kuti: “‘Ngati kumwamba kungayezedwe ndipo ngati maziko a dziko lapansi angafufuzidwe, ndiye kuti inenso ndingakane mbadwa zonse za Isiraeli chifukwa cha zonse zimene achita,’ akutero Yehova.”+
-