Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • Salimo 76:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  7 Inu nokha ndinu wochititsa mantha.+

      Ndi ndani angapirire mkwiyo wanu waukulu?+

  • Yeremiya 50:44-46
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 44 Taona! Wina adzabwera ngati mkango kuchokera munkhalango zowirira zamʼmphepete mwa Yorodano. Adzabwera kudzaukira malo otetezeka odyetserako ziweto, koma mʼkanthawi kochepa ndidzawathamangitsa* pamalowo. Ndidzaika pamalopo mtsogoleri amene ndamusankha.+ Chifukwa ndi ndani amene angafanane ndi ine ndipo ndi ndani angatsutsane nane? Kodi pali mʼbusa amene angakane kuchita zimene ine ndikufuna?+ 45 Tsopano amuna inu, tamverani zimene Yehova wasankha* kuchitira Babulo+ ndiponso zimene waganiza kuti achitire dziko la Akasidi.

      Ndithudi, chilombo chidzakokera kutali ana a nkhosa.

      Adzachititsa kuti malo awo okhala asanduke bwinja chifukwa cha zimene anthuwo anachita.+

      46 Phokoso limene lidzamveke Babulo akadzagwidwa lidzachititsa kuti dziko lapansi ligwedezeke,

      Ndipo kulira kudzamveka pakati pa mitundu ya anthu.”+

  • Nahumu 1:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  6 Iye atapsa mtima, ndani angaime pamaso pake?+

      Iye atakwiya, ndani angalimbe mtima kuima pamaso pake?+

      Mkwiyo wake adzaukhuthula ngati moto,

      Ndipo miyala idzaphwanyidwa chifukwa cha iye.

Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • tumizirani
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • zachinsinsi
  • JW.ORG
  • Lowani
tumizirani