-
Yeremiya 50:44-46Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
44 Taona! Wina adzabwera ngati mkango kuchokera munkhalango zowirira zamʼmphepete mwa Yorodano. Adzabwera kudzaukira malo otetezeka odyetserako ziweto, koma mʼkanthawi kochepa ndidzawathamangitsa* pamalowo. Ndidzaika pamalopo mtsogoleri amene ndamusankha.+ Chifukwa ndi ndani amene angafanane ndi ine ndipo ndi ndani angatsutsane nane? Kodi pali mʼbusa amene angakane kuchita zimene ine ndikufuna?+ 45 Tsopano amuna inu, tamverani zimene Yehova wasankha* kuchitira Babulo+ ndiponso zimene waganiza kuti achitire dziko la Akasidi.
Ndithudi, chilombo chidzakokera kutali ana a nkhosa.
Adzachititsa kuti malo awo okhala asanduke bwinja chifukwa cha zimene anthuwo anachita.+
46 Phokoso limene lidzamveke Babulo akadzagwidwa lidzachititsa kuti dziko lapansi ligwedezeke,
Ndipo kulira kudzamveka pakati pa mitundu ya anthu.”+
-