-
Yeremiya 39:4-7Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
4 Mfumu Zedekiya ya Yuda ndi asilikali onse ataona adaniwo, anathawira+ kunja kwa mzinda usiku. Iwo anadzera njira yakumunda wa mfumu nʼkukadutsa pageti limene linali pakati pa makoma awiri ndipo anapitiriza kuthawa kulowera ku Araba.+ 5 Koma asilikali a Akasidi anawathamangitsa ndipo Zedekiya anamupeza mʼchipululu cha Yeriko.+ Anamugwira nʼkupita naye kwa Mfumu Nebukadinezara* ya Babulo ku Ribila,+ mʼdziko la Hamati,+ kumene Nebukadinezara anamuweruza. 6 Zitatero mfumu ya Babulo inapha ana aamuna a Zedekiya ku Ribila, Zedekiyayo akuona. Inaphanso anthu onse olemekezeka a ku Yuda.+ 7 Mfumu ya Babulo inachititsa khungu maso a Zedekiya ndipo kenako inamumanga mʼmaunyolo akopa* kuti apite naye ku Babulo.+
-