Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • Yesaya 1:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Yehova wanena kuti: “Kodi nsembe zanu zambirimbirizo zili ndi phindu lanji kwa ine?+

      Nsembe zanu zopsereza za nkhosa zamphongo+ ndiponso mafuta a nyama zodyetsedwa bwino+ zandikwana.

      Sindikusangalala ndi magazi+ a ngʼombe zazingʼono zamphongo,+ a ana a nkhosa ndiponso magazi a mbuzi.+

  • Yesaya 66:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  3 Munthu amene akupha ngʼombe yamphongo ali ngati amene akupha munthu.+

      Amene akupereka nsembe ya nkhosa ali ngati amene akuthyola khosi la galu.+

      Munthu amene akupereka mphatso ali ngati amene akupereka magazi a nkhumba.+

      Amene akupereka nsembe yachikumbutso ya lubani+ ali ngati munthu amene akupereka dalitso pogwiritsa ntchito mawu onenerera zamatsenga.*+

      Anthuwo asankha njira zawozawo,

      Ndipo amasangalala ndi zinthu zonyansa.

  • Yeremiya 7:21
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 21 Yehova wa magulu ankhondo akumwamba, Mulungu wa Isiraeli, wanena kuti, ‘Wonjezerani nsembe zanu zopsereza zathunthu pansembe zanu zinazo ndipo muzidye nokha.+

  • Amosi 5:21
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 21 Ine ndimadana ndi zikondwerero zanu ndipo sindigwirizana nazo,+

      Komanso sindisangalala ndi fungo la nsembe zanu zoperekedwa pamisonkhano yanu yapadera.

Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • tumizirani
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • zachinsinsi
  • JW.ORG
  • Lowani
tumizirani