Salimo
3 Nyadirani dzina lake loyera.+
Mitima ya anthu ofunafuna Yehova isangalale.+
4 Funafunani Yehova+ ndipo muzidalira mphamvu zake.
Nthawi zonse muzimupempha kuti akuthandizeni.*
5 Kumbukirani ntchito zodabwitsa zimene wachita,
Kumbukirani zozizwitsa zake ndi ziweruzo zimene wapereka,+
6 Inu mbadwa* za Abulahamu mtumiki wake,+
Inu ana a Yakobo, osankhidwa ake.+
7 Iye ndi Yehova Mulungu wathu.+
Ziweruzo zake zili padziko lonse lapansi.+
8 Amakumbukira pangano lake mpaka kalekale,+
Lonjezo limene anapereka* ku mibadwo 1,000.+
9 Wakumbukira pangano limene anapangana ndi Abulahamu,+
Komanso lumbiro limene analumbira kwa Isaki,+
10 Limene analikhazikitsa monga lamulo kwa Yakobo,
Komanso monga pangano lokhalapo mpaka kalekale kwa Isiraeli,
11 Pamene anati, “Ndidzakupatsa dziko la Kanani+
Kuti likhale cholowa chako.”+
12 Pamene ananena zimenezi, nʼkuti iwo ali ochepa.+
Nʼkuti ali ochepa kwambiri komanso ali alendo mʼdzikolo.+
13 Iwo ankayendayenda kuchokera ku mtundu wina kupita ku mtundu wina,
Komanso kuchokera mu ufumu wina kupita kwa anthu a mtundu wina.+
14 Mulungu sanalole kuti munthu aliyense awapondereze,+
Koma anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo.+
15 Iye anati: “Musakhudze odzozedwa anga,
Ndipo aneneri anga musawachitire choipa chilichonse.”+
17 Mulungu anatsogoza Yosefe,
Munthu amene anagulitsidwa kuti akhale kapolo.+
18 Kumeneko anamanga* mapazi ake mʼmatangadza,+
Khosi lake analiika mʼzitsulo
19 Mpaka nthawi imene zimene Mulungu ananena zinakwaniritsidwa,+
Mawu a Yehova ndi amene anamuyenga.
20 Mfumu inalamula kuti amutulutse mʼndende,+
Wolamulira mitundu ya anthu anatulutsa Yosefe mʼndende.
21 Anamupatsa udindo woyangʼanira banja lake
Komanso woyangʼanira chuma chake chonse.+
22 Anamupatsa mphamvu zolamulira* akalonga ake mmene akufunira
Komanso kuti akuluakulu aziwaphunzitsa zinthu za nzeru.+
23 Kenako Isiraeli anapita ku Iguputo+
Ndipo Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
24 Mulungu anachititsa kuti anthu ake aberekane kwambiri,+
Iye anawachititsa kuti akhale amphamvu kwambiri kuposa adani awo.+
25 Analola adaniwo kuti asinthe mitima yawo nʼkuyamba kudana ndi anthu ake,
Komanso kukonzera chiwembu atumiki akewo.+
27 Iwowa anachita zizindikiro za Mulungu pamaso pa Aiguputo,
Anachita zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.+
29 Anasandutsa madzi a Aiguputo kukhala magazi,
Ndipo anapha nsomba zawo.+
30 Mʼdziko lawo munadzaza achule,+
Ngakhalenso mʼzipinda za mafumu awo.
31 Analamula kuti pagwe ntchentche zoluma,
Komanso tizilombo touluka toyamwa magazi,* mʼmadera awo onse.+
33 Anawononga mitengo yawo ya mpesa ndi ya mkuyu
Ndipo anakhadzula mitengo mʼdziko lawo.
34 Analamula kuti pagwe dzombe,
Dzombe lingʼonolingʼono losawerengeka.+
35 Dzombelo linadya zomera zonse mʼdziko lawo,
Linadyanso mbewu zonse zamʼmunda mwawo.
36 Kenako Mulungu anapha mwana aliyense woyamba kubadwa mʼdziko lawo,+
Chiyambi cha mphamvu zawo zobereka.
37 Anatulutsa anthu ake atatenga siliva ndi golide.+
Ndipo pakati pa mafuko ake panalibe amene anapunthwa panjira.
38 Aiguputo anasangalala Aisiraeli atatuluka mʼdzikolo,
Chifukwa ankawaopa kwambiri.+
39 Mulungu anatumiza mtambo kuti uwateteze+
Komanso moto kuti uziwaunikira usiku.+
41 Anatsegula thanthwe ndipo panatuluka madzi ambiri.+
Madziwo anayenda ngati mtsinje kudutsa mʼchipululu.+
42 Chifukwa iye anakumbukira lonjezo lake loyera limene analonjeza mtumiki wake Abulahamu.+
43 Choncho Mulungu anatulutsa anthu ake mʼdzikomo anthuwo akusangalala,+
Anatulutsa osankhidwa ake akufuula mokondwera.
44 Anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina,+
Anatenga zinthu zimene mitundu ina ya anthu inapeza itagwira ntchito mwakhama,+
45 Anachita zimenezi kuti asunge malangizo ake,+
Komanso kusunga malamulo ake.
Tamandani Ya!*