Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • ll section 7
  • Kodi Yesu Anali Ndani?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Yesu Anali Ndani?
  • Mverani Mulungu Kuti Mudzapeze Moyo Wosatha
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Yesu Khristu Ndi Ndani?
    Zimene Baibulo Limaphunzitsa
  • Kodi Yesu Khristu Ndani?
    Uthenga Wabwino Wochokera kwa Mulungu
  • N’chifukwa Chiyani Baibulo Limati Yesu Ndi Mwana wa Mulungu?
    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
Mverani Mulungu Kuti Mudzapeze Moyo Wosatha
ll section 7

CHIGAWO 7

Kodi Yesu Anali Ndani?

Yehova anatumiza Yesu padziko lapansi. 1 Yohane 4:9

Yesu ali kudzanja lamanja la Mulungu kumwamba

Ngati tikufuna kukondweretsa Yehova, tiyenera kumvera munthu winanso wofunika kwambiri. Kale kwambiri Yehova asanalenge Adamu, analenga mngelo wamphamvu kwambiri kumwamba.

Mariya ali woyembekezera komanso Yesu atabadwa

Patapita nthawi, Yehova anatumiza mngelo ameneyu kudzabadwa ngati mwana ku Betelehemu kwa namwali wina dzina lake Mariya. Mwana ameneyo anam’patsa dzina lakuti Yesu.​—Yohane 6:38.

Yesu akuphunzitsa anthu za Yehova

Ali padziko lapansi, Yesu anasonyeza bwino kwambiri makhalidwe a Mulungu. Iye anali wachifundo, wachikondi ndiponso anthu ankafika kwa iye momasuka. Ankaphunzitsa anthu choonadi chonena za Yehova mopanda mantha.

Yesu ankachita zinthu zabwino koma anthu ankadana naye. 1 Petulo 2:21-24

Yesu akuukitsa kamtsikana komanso kuchiritsa munthu

Yesu anachiritsanso odwala ndi kuukitsa anthu ena amene anafa.

Atsogoleri a chipembedzo ankadana ndi Yesu chifukwa iye ankaulula zochita zawo zoipa ndipo ankaululanso kuti iwo ankaphunzitsa zinthu zabodza.

Yesu akumenyedwa kenako kuphedwa

Atsogoleri a chipembedzo anachititsa Aroma kuti amenye ndi kupha Yesu.

  • N’chifukwa chiyani tiyenera kuphunzira za Yesu?​—Yohane 17:3.

  • Kodi Yesu ankachita chiyani kumwamba asanabwere padziko lapansi?​—Akolose 1:15-17.

    Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
    • tumizirani
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • zachinsinsi
    • JW.ORG
    • Lowani
    tumizirani