Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • ll section 9
  • Kodi Paradaiso Adzabwera Liti?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Paradaiso Adzabwera Liti?
  • Mverani Mulungu Kuti Mudzapeze Moyo Wosatha
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Dzikoli Lithadi Posachedwa?
    Zimene Baibulo Limaphunzitsa
  • Kodi Mapeto Adzafika Liti? Zimene Yesu Ananena
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2021
  • Kodi Chizindikiro cha “Masiku Otsiriza” Kapena Kuti ‘Nthawi ya Mapeto’ N’chiyani?
    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Kodi Tiyenera Kukonda Ndani Kuti Tikhale Osangalala?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2018
Mverani Mulungu Kuti Mudzapeze Moyo Wosatha
ll section 9

CHIGAWO 9

Kodi Paradaiso Adzabwera Liti?

Mavuto amene akuchitika padzikoli akusonyeza kuti posachedwapa, Ufumu wa Mulungu uyamba kulamulira padziko lapansi. Luka 21:10, 11; 2 Timoteyo 3:1-5

Mavuto a m’masiku otsiriza—juga, nkhondo, matenda, njala, kusamvera makolo, nkhanza za m’banja

Baibulo linaneneratu zinthu zambiri zimene zikuchitika masiku ano. Linaneneratu kuti anthu adzakhala okonda ndalama, osamvera makolo, oopsa ndiponso okonda zosangalatsa.

Linanenanso kuti kudzakhala zivomezi zamphamvu, nkhondo, njala ndiponso miliri. Zinthu zimenezi zikuchitika masiku ano.

Wa Mboni za Yehova akulalikira uthenga wabwino

Yesu ananenanso kuti uthenga wabwino wonena za Ufumu udzalalikidwa padziko lonse lapansi.​—Mateyu 24:14.

Ufumu umenewu udzachotsa zinthu zonse zoipa. 2 Petulo 3:13

Anthu oipa awonongedwa pa Aramagedo ndipo Satana ndi ziwanda zake alangidwa

Posachedwapa, Yehova awononga anthu oipa.

Satana ndi ziwanda zake adzalangidwa.

Yesu wakhala pampando kumwamba ndipo anthu amitundu yosiyanasiyana akusangalala

Anthu amene amamvera Mulungu adzapulumuka n’kulowa m’dziko latsopano lolungama. M’dziko limeneli anthu adzakhala mopanda mantha ndipo azidzakhulupirirana ndi kukondana kwambiri.

  • Kodi Yesu ananena kuti chidzachitike n’chiyani m’nthawi yathu ino?​—Mateyu 24:3-14.

  • Anthu oipa adzawonongedwa.—2 Petulo 3:7.

    Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
    • tumizirani
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • zachinsinsi
    • JW.ORG
    • Lowani
    tumizirani