Mawu a M'munsi
a Ngakhale kuti m’dzikoli tingakumane ndi mavuto osayembekezereka, tingakhale otsimikiza kuti Yehova adzathandiza atumiki ake okhulupirika. Ndiye kodi Yehova anathandiza bwanji atumiki ake m’mbuyomo? Nanga kodi amatithandiza bwanji masiku ano? Kukambirana zitsanzo za anthu otchulidwa m’Baibulo komanso a masiku ano kungatithandize kuti tizimudalira kwambiri kuti nafenso adzatithandiza.