Mawu a M'munsi
a Timalimbikitsana tikamayankha pamisonkhano. Komabe ena amachita mantha kupereka ndemanga. Ena amakonda kupereka ndemanga koma amafuna kuti azitchulidwa pafupipafupi. Mulimonse mmene zingakhalire, kodi tingasonyeze bwanji kuti timaganizirana n’cholinga choti aliyense azilimbikitsidwa? Nanga kodi tingatani kuti tizipereka ndemanga zomwe zingalimbikitse abale ndi alongo athu pa chikondi ndi ntchito zabwino? Nkhaniyi ifotokoza zimenezi.