Mawu a M'munsi
a Ngakhale Yobu, yemwe anali wokhulupirika, anasokonezeka ataganizira mmene anzake atatu ankamuonera. Poyamba, ana ake onse atamwalira komanso katundu wake yense atawonongeka, “Yobu sanachimwe kapena kuimba Mulungu mlandu woti wachita zinthu zoipa.” (Yobu 1:22; 2:10) Koma pambuyo pake, anzakewo atamunena kuti Yobu wachita zinazake zoipa, anayamba ‘kulankhula mosaganiza bwino.’ Iye ankaona kuti chofunika kwambiri ndi kuteteza mbiri yake kuposa kuyeretsa dzina la Mulungu.—Yobu 6:3; 13:4, 5; 32:2; 34:5.