Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • sjj 76
  • Kodi Mumamva Bwanji?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Mumamva Bwanji?
  • Imbirani Yehova Mosangalala
  • Nkhani Yofanana
  • Yehova Akutipempha Kuti: “Mwana Wanga, Khala Wanzeru”
    Imbirani Yehova Mosangalala
  • “Muzitsimikizira Kuti Zinthu Zofunika Kwambiri Ndi Ziti”
    Imbirani Yehova Mosangalala
  • Tadzipereka kwa Mulungu
    Imbirani Yehova Mosangalala
  • Malo Amene Adzachititsa Kuti Mulemekezedwe
    Imbirani Yehova Mosangalala
Onani Zambiri
Imbirani Yehova Mosangalala
sjj 76

NYIMBO 76

Kodi Mumamva Bwanji?

zosindikizidwa

(Aheberi 13:15)

  1. 1. Kodi m’mamva bwanji

    Mukasonyeza khama

    Polalikira anthu

    Ndi kuwaphunzitsa?

    Mukamayesetsa

    M’lungu adzadalitsa.

    Mudzathandiza anthu

    Kudziwa Mulungu.

    (KOLASI)

    Timasangalala ndithu

    Kupereka mtima wathu,

    Choncho timutumikire

    Tsiku lililonse.

  2. 2. Kodi m’mamva bwanji

    Mukadziwatu kuti

    Mwawafika pamtima

    Akamva uthenga?

    Ena amakana,

    Ena amatitsutsa.

    Koma timanyadira

    Tikalalikira.

    (KOLASI)

    Timasangalala ndithu

    Kupereka mtima wathu,

    Choncho timutumikire

    Tsiku lililonse.

  3. 3. Kodi m’mamva bwanji

    Pokumbukira kuti

    Mwa chikondi Yehova

    Amatsogolera?

    Timalalikira,

    Timaphunzitsa anthu

    Akhale ndi tsogolo,

    Adzapeze moyo.

    (KOLASI)

    Timasangalala ndithu

    Kupereka mtima wathu,

    Choncho timutumikire

    Tsiku lililonse.

(Onaninso Mac. 13:48; 1 Ates. 2:4; 1 Tim. 1:​11.)

    Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
    • tumizirani
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • zachinsinsi
    • JW.ORG
    • Lowani
    tumizirani