LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • ijwbq nkhani 29
  • Kodi Niyenela Kupemphela kwa Oyela Mtima?

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kodi Niyenela Kupemphela kwa Oyela Mtima?
  • Kuyankha Mafunso Okhudza Baibo
  • Tumitu
  • Nkhani Zofanana
  • Yankho la m’Baibo
  • Kodi Tiyenela Kupemphela kwa Yesu?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • Muyandikileni Mulungu Kupitila m’Pemphelo
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
  • Mwayi Wa Pemphelo
    Zimene Baibulo Ingatiphunzitse
  • Kodi Yehova Amamvetsela kwa Ife?
    Mvetselani kwa Mulungu Kuti Mukhale ndi Moyo Wamuyaya
Onaninso Zina
Kuyankha Mafunso Okhudza Baibo
ijwbq nkhani 29

Kodi Niyenela Kupemphela kwa Oyela Mtima?

Yankho la m’Baibo

Ayi. Baibo imaonetsa kuti tiyenela kupemphela kwa Mulungu yekha, m’dzina la Yesu. Yesu anauza ophunzila ake kuti: “Cifukwa cake pemphelani inu comweci: Atate wathu wa Kumwamba, Dzina lanu liyeletsedwe.” (Mateyu 6:9, Buku Lopatulika Ndilo Mau a Mulungu) Iye sanalangizepo ophunzila ake kuti azipemphela kwa oyela mtima, angelo, kapena munthu wina aliyense, koma kwa Mulungu cabe.

Yesu anauzanso ophunzila ake kuti: “Ine ndine njila, coonadi ndi moyo. Palibe amene amafika kwa Atate osadzela mwa ine.” (Yohane 14:6) Ndipo Mulungu anasakha Yesu yekha kuti tizipeleka mapemphelo athu kupitila mwa iye.—Aheberi 7:25.

Nanga bwanji ngati nimapemphela kwa Mulungu komanso kwa oyela mtima?

Mu Malamulo Khumi amene Mulungu anapatsa anthu ake, iye anakamba kuti: “Ine Yehova Mulungu wako ndili Mulungu wansanje.” (Ekisodo 20:5,) Kodi Mulungu ni “wansanje” m’njila yotani? Iye amafuna kuti tizilambila iye yekha na kudzipeleka kwa iye. Komanso, amafuna kuti tizipemphela kwa iye yekhabasi.—Yesaya 48:11.

Conco, timalakwila Mulungu ngati tipemphela kwa munthu winawake, ngakhale oyela mtima, kapenanso angelo oyela. Pamene mtumwi Yohane anafuna kulambila mngelo, mngeloyo anam’letsa n’kumuuza kuti: “Usatelo ayi! Inetu ndangokhala kapolo mnzako, ndi wa abale ako amene ali ndi nchito yocitila umboni za Yesu. Lambila Mulungu”—Chivumbulutso 19:10.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani