1 Mbiri
5 Ana a Yafeti anali Gomeri, Magogi,+ Madai,+ Yavani,+ Tubala, Meseke,+ ndi Tirasi.+
6 Ana a Gomeri anali Asikenazi,+ Rifati,+ ndi Togarima.+
7 Ana a Yavani anali Elisaha,+ Tarisi,+ Kitimu,+ ndi Rodanimu.+
8 Ana a Hamu anali Kusi,+ Miziraimu,+ Puti,+ ndi Kanani.+
9 Ana a Kusi anali Seba,+ Havila, Sabita,+ Raama,+ ndi Sabiteka.+
Ana a Raama anali Sheba ndi Dedani.+
10 Kusi anabereka Nimurodi+ amene anali woyamba kukhala wamphamvu padziko lapansi.+
11 Miziraimu anabereka Ludimu,+ Anamimu, Lehabimu, Nafituhimu,+ 12 Patirusimu,+ ndi Kasiluhimu+ (Afilisiti+ anachokera mwa iyeyu), ndiponso Kafitorimu.+
13 Kanani anabereka Sidoni+ mwana wake woyamba, kenako anabereka Heti.+ 14 Anaberekanso Ayebusi,+ Aamori,+ Agirigasi,+ 15 Ahivi,+ Aariki, Asini,+ 16 Aarivadi,+ Azemari,+ ndi Ahamati.+
18 Aripakisadi anabereka Shela,+ ndipo Shela anabereka Ebere.+
19 Ebere anabereka ana awiri. Wina dzina lake anali Pelegi,*+ chifukwa m’masiku ake, dziko lapansi linagawikana. M’bale wakeyo dzina lake anali Yokitani.
20 Yokitani anabereka Alamodadi, Selefi, Hazaramaveti, Yera,+ 21 Hadoramu, Uzali, Dikila,+ 22 Obali, Abimaele, Sheba,+ 23 Ofiri,+ Havila,+ ndi Yobabi.+ Onsewa anali ana a Yokitani.
28 Ana a Abulahamu anali Isaki+ ndi Isimaeli.+
29 Awa ndiwo mabanja awo: Nebayoti,+ mwana woyamba wa Isimaeli, Kedara,+ Adibeele, Mibisamu,+ 30 Misima, Duma,+ Maasa, Hadadi,+ Tema, 31 Yeturi, Nafisi, ndi Kedema.+ Amenewa ndiwo anali ana a Isimaeli.
32 Ketura+ mdzakazi*+ wa Abulahamu anabereka Zimirani, Yokesani, Medani,+ Midiyani,+ Isibaki,+ ndi Shuwa.+
Ana a Yokesani anali Sheba ndi Dedani.+
33 Ana a Midiyani anali Efa,+ Eferi, Hanoki, Abida, ndi Elida.+
Onsewa anali ana aamuna a Ketura.
34 Abulahamu anabereka Isaki.+ Ana a Isaki anali Esau+ ndi Isiraeli.+
35 Ana a Esau anali Elifazi, Reueli,+ Yeusi, Yalamu, ndi Kora.+
36 Ana a Elifazi anali Temani,+ Omari, Zefo, Gatamu, Kenazi,+ Timina,+ ndi Amaleki.+
37 Ana a Reueli anali Nahati, Zera, Shama, ndi Miza.+
38 Ana a Seiri+ anali Lotani, Sobala, Zibeoni, Ana,+ Disoni, Ezeri, ndi Disani.+
39 Ana a Lotani anali Hori ndi Homamu. Mlongo wake wa Lotani anali Timina.+
40 Ana a Sobala anali Alivani, Manahati, Ebala, Sefo, ndi Onamu.+
Ana a Zibeoni anali Aya ndi Ana.+
41 Mwana* wa Ana anali Disoni.+
Ana a Disoni anali Hemadani, Esibani, Itirani, ndi Kerana.+
42 Ana a Ezeri+ anali Bilihani, Zavani, ndi Ekani.+
Ana a Disani anali Uzi ndi Arani.+
43 Tsopano awa ndiwo mafumu amene analamulira dziko la Edomu+ ana a Isiraeli asanayambe kulamulidwa ndi mfumu ina iliyonse:+ Bela mwana wa Beori. Dzina la mzinda wake linali Dinihaba.+ 44 Patapita nthawi, Bela anamwalira ndipo Yobabi mwana wa Zera+ wa ku Bozira,+ anayamba kulamulira m’malo mwake. 45 Patapita nthawi, Yobabi anamwalira ndipo Husamu+ wa kudziko la Atemani,+ anayamba kulamulira m’malo mwake. 46 Patapita nthawi, Husamu anamwalira ndipo Hadadi+ mwana wa Bedadi, amene anagonjetsa Amidiyani+ m’dziko la Mowabu, anayamba kulamulira m’malo mwake. Dzina la mzinda wake linali Aviti.+ 47 Patapita nthawi, Hadadi anamwalira ndipo Samila wa ku Masereka+ anayamba kulamulira m’malo mwake. 48 Patapita nthawi, Samila anamwalira ndipo Shauli wa ku Rehoboti+ mzinda wa m’mphepete mwa Mtsinje,* anayamba kulamulira m’malo mwake. 49 Patapita nthawi, Shauli anamwalira ndipo Baala-hanani mwana wa Akibori+ anayamba kulamulira m’malo mwake. 50 Patapita nthawi, Baala-hanani anamwalira ndipo Hadadi anayamba kulamulira m’malo mwake. Dzina la mzinda wake linali Pau, ndipo mkazi wake dzina lake linali Mehetabele mwana wa Matiredi mwana wamkazi wa Mezahabu.+ 51 Patapita nthawi, Hadadi anamwalira.
Mafumu a Edomu anali mfumu Timina, mfumu Aliva, mfumu Yeteti,+ 52 mfumu Oholibama, mfumu Ela, mfumu Pinoni,+ 53 mfumu Kenazi, mfumu Temani, mfumu Mibezari,+ 54 mfumu Magidieli, ndi mfumu Iramu.+ Amenewa ndiwo anali mafumu+ a Edomu.