Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Takulandirani.
Laibulaleyi imathandiza anthu kufufuza mabuku ofalitsidwa ndi Mboni za Yehova a m'zinenero zosiyanasiyana.
Kuti mupange dawunilodi mabuku, pitani pa jw.org.
Chilengezo
Chinenero chatsopano chomwe chilipo: Mbum
  • Lero

Lolemba, July 28

Amene ali wogwirizana ndi inu ndi wamkulu kuposa amene ali wogwirizana ndi dziko.​—1 Yoh. 4:4.

Mukamachita mantha, muziganizira zimene Yehova adzachite m’tsogolo, Satana akadzachotsedwa. Pamsonkhano wachigawo wa 2014, panali chitsanzo cha zimene tingachite poganizira za chiyembekezo chathu. Mu chitsanzocho, bambo ankakambirana ndi banja lake mmene lemba la 2 Timoteyo 3:1-5 lingamvekere ngati mavesiwa atakhala kuti akufotokoza mmene zidzakhalire m’Paradaiso. Anawerenga kuti: “M’dziko latsopano, idzakhala nthawi yapadera komanso yosangalatsa. Pakuti anthu adzakhala okonda anzawo, okonda kulambira Mulungu, odzichepetsa, ofatsa, otamanda Mulungu, omvera makolo, oyamikira, okhulupirika, okonda achibale awo, ofuna kugwirizana ndi anzawo, onena zabwino za anzawo, odziletsa, odekha, okonda zabwino, odalirika, oganizira za ena, osadzitukumula ndiponso osanyada, okonda Mulungu, m’malo mokonda zosangalatsa, ndiponso odziperekadi kwa Mulungu. Anthu amenewa usasiyane nawo.” Kodi mumakambirana ndi anthu a m’banja lanu kapena anzanu mmene moyo udzakhalire m’dziko latsopano? w24.01 6 ¶13-14

Kuphunzira Malemba Tsiku ndi Tsiku—2025

Lachiwiri, July 29

Umandisangalatsa kwambiri.—Luka 3:22.

N’zolimbikitsa kwambiri kudziwa kuti Yehova amasangalala ndi anthu ake onse monga gulu. Baibulo limati: “Yehova amasangalala ndi anthu ake.” (Sal. 149:4) Komabe nthawi zina ena angamakayikire n’kumadzifunsa kuti, ‘Kodi Yehova amasangalala ndi ineyo pandekha?’ Ambiri mwa atumiki okhulupirika a Yehova akale nthawi zinanso ankavutika ndi maganizo ngati amenewa. (1 Sam. 1:6-10; Yobu 29:2, 4; Sal. 51:11) Baibulo limasonyeza kuti anthu omwe si angwiro akhoza kusangalatsa Yehova. Kodi tingachite bwanji zimenezi? Tiyenera kukhulupirira Yesu Khristu komanso kubatizidwa. (Yoh. 3:16) Tikatero timasonyeza poyera kuti talapa machimo athu ndipo talonjeza kuti tizichita zimene Mulungu amafuna. (Mac. 2:38; 3:19) Yehova amasangalala akaona tikuchita zimenezi n’cholinga choti tikhale naye pa ubwenzi. Iye amasangalala nafe n’kumationa ngati anzake apamtima tikamapitiriza kuchita zimene tingathe pokwaniritsa zimene tinalonjeza podzipereka.—Sal. 25:14. w24.03 26 ¶1-2

Kuphunzira Malemba Tsiku ndi Tsiku—2025

Lachitatu, July 30

Ife sitingasiye kulankhula za zinthu zimene tinaziona ndi kuzimva.​—Mac. 4:20.

Tingatsanzire ophunzira a Yesu, popitiriza kulalikira ngakhale pamene akuluakulu a boma aletsa ntchito yathu. Ifenso tingakhale otsimikiza kuti Yehova adzatithandiza kuti tikwaniritse utumiki wathu. Choncho tizimupempha kuti atithandize kukhala olimba mtima komanso atipatse nzeru. Tizimupemphanso kuti atithandize kupirira mavuto. Ambirife tikukumana ndi mavuto okhudza thanzi kapena maganizo, imfa ya okondedwa athu, mavuto a m’banja, kuzunzidwa kapenanso mavuto ena. Ndipo zinthu monga miliri komanso nkhondo zachititsa kuti zikhale zovuta kwambiri kulimbana ndi mavutowa. Choncho muzipemphera kwa Yehova mochokera pansi pa mtima. Muzimuuza zimene zikuchitika pa moyo wanu ngati mmene mungachitire ndi mnzanu wapamtima. Muzikhulupirira kuti Yehova “adzachitapo kanthu.” (Sal. 37:3, 5) Kulimbikira kupemphera kungatithandize ‘kupirira mavuto.’ (Aroma 12:12) Yehova amadziwa zimene zikuchitikira atumiki ake ndipo ‘amamva kufuula kwawo kopempha thandizo.’—Sal. 145:18, 19. w23.05 5-6 ¶12-15

Kuphunzira Malemba Tsiku ndi Tsiku—2025
Takulandirani.
Laibulaleyi imathandiza anthu kufufuza mabuku ofalitsidwa ndi Mboni za Yehova a m'zinenero zosiyanasiyana.
Kuti mupange dawunilodi mabuku, pitani pa jw.org.
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena