Numeri
21 Tsopano mfumu ya Akanani ya ku Aradi+ yomwe inali kukhala ku Negebu,+ inamva kuti Aisiraeli akubwera kudzera njira ya ku Atarimu. Itamva zimenezo inapita kukamenyana nawo ndipo Aisiraeli ena inawagwira ndi kupita nawo kudziko lake. 2 Aisiraeli ataona zimenezo, analonjeza kwa Yehova kuti:+ “Mukapereka anthuwa m’manja mwathu, ndithu ifenso tidzawononga mizinda yawo.”+ 3 Yehova anamva mawu a Aisiraeli, ndipo anapereka Akananiwo m’manja mwawo. Aisiraeli anawononga Akananiwo limodzi ndi mizinda yawo. N’chifukwa chake malowo anawatcha Horima.*+
4 Pamene Aisiraeliwo anali pa ulendo kuchokera kuphiri la Hora+ kudzera njira yopita ku Nyanja Yofiira, kulambalala dziko la Edomu,+ anayamba kutopa chifukwa cha njirayo. 5 Choncho iwo anayamba kuwiringula kwa Mulungu+ ndiponso Mose,+ kuti: “Munatitulutsiranji m’dziko la Iguputo? Kodi mumafuna kuti tidzafere m’chipululu?+ Kuno chakudya kulibe, madzinso kulibe.+ Chakudya chonyansachi chafika potikola.”+ 6 Pamenepo Yehova anatumiza njoka zapoizoni pakati pawo,+ ndipo zinayamba kuwaluma moti Aisiraeli ambiri anafa.+
7 Anthuwo ataona zimenezo, anapita kwa Mose n’kumuuza kuti: “Tachimwa ife,+ chifukwa talankhula mowiringula kwa Yehova ndiponso kwa inuyo. Tipepesereni kwa Yehova kuti atichotsere njokazi.”+ Pamenepo Mose anayamba kuwapepesera kwa Mulungu.+ 8 Ndiyeno Yehova anauza Mose kuti: “Upange chifanizo cha njoka yapoizoni* ndipo uchiike pamtengo wachizindikiro. Munthu aliyense amene walumidwa, akayang’ana njokayo akhalebe ndi moyo.”+ 9 Pamenepo Mose anapanga njoka yamkuwa+ ndi kuiika pamtengo wachizindikirowo.+ Ndipo zinachitikadi kuti munthu akalumidwa ndi njoka n’kuyang’ana+ njoka yamkuwayo, anali kukhalabe ndi moyo.+
10 Pambuyo pake, ana a Isiraeli anasamuka n’kukamanga msasa ku Oboti.+ 11 Kenako anasamuka ku Oboti n’kukamanga msasa ku Iye-abarimu,+ m’chipululu choyang’anana ndi dziko la Mowabu, kotulukira dzuwa. 12 Atachoka kumeneko anakamanga msasa m’chigwa* cha Zeredi.+ 13 Atasamuka kumeneko anakamanga msasa m’dera la chigwa cha Arinoni,+ m’chipululu chochokera kumalire a dziko la Aamori. Chigwa cha Arinoni chinali malire pakati pa dziko la Mowabu ndi la Aamori. 14 N’chifukwa chake buku la Nkhondo za Yehova limati:
“Vahebi ku Sufa, ndi zigwa* za Arinoni. 15 Mitsinje ya m’zigwazo imakafika ku Ari+ ndipo imayenda m’malire a dziko la Mowabu.”
16 Atachoka kumeneko anapita ku Beere.+ Kumeneku ndi kuchitsime kumene Yehova anauza Mose kuti: “Sonkhanitsa anthuwo kuti ndiwapatse madzi.”+
17 Pa nthawi imeneyo Aisiraeli anaimba nyimbo+ yakuti:
“Tumphuka, chitsime iwe! Vomerezani nyimboyo, anthu inu!
18 Chitsimechi n’chokumbidwa ndi akalonga. Chofukula anthu olemekezeka,
Chofukula ndi ndodo ya mtsogoleri wa asilikali,+ chofukula ndi ndodo zawo.”
Atachoka kuchipululucho anafika ku Matana. 19 Atachoka ku Matana anafika ku Nahaliyeli, ndipo atachoka ku Nahaliyeli anafika ku Bamoti.+ 20 Atachoka ku Bamoti anafika kuchigwa cha dziko la Mowabu,+ kumalire ndi mzinda wa Pisiga.+ Chitunda cha Pisiga chinayang’anana ndi dera la Yesimoni.+
21 Tsopano Aisiraeli anatuma amithenga kupita kwa Sihoni+ mfumu ya Aamori kukanena kuti: 22 “Tiloleni tidzere m’dziko lanu. Sitipatukira pamunda uliwonse, kapena pamunda wa mpesa. Sitimwa madzi pachitsime chilichonse. Tizingoyenda mumsewu wa mfumu mpaka titadutsa m’dziko lanu.”+ 23 Koma Sihoni sanalole kuti Aisiraeli adzere m’dziko lake.+ M’malomwake, iye anasonkhanitsa anthu ake onse n’kupita kukamenyana ndi Aisiraeli m’chipululumo. Anakafika ku Yahazi,+ kumene anayamba kumenyana ndi Aisiraeli. 24 Koma Aisiraeli anapha anthuwo ndi lupanga+ n’kuwalanda dziko lawo,+ kuyambira kuchigwa cha Arinoni+ mpaka kuchigwa cha Yaboki,+ pafupi ndi ana a Amoni, chifukwa Yazeri+ ali kumalire kwa ana a Amoni.+
25 Choncho Aisiraeli analanda mizinda yonseyi n’kuyamba kukhala m’mizinda yonse ya Aamori+ ku Hesiboni,+ ndi m’midzi yake yonse yozungulira. 26 Anayamba kukhala kumeneko chifukwa Hesiboni unali mzinda wa Sihoni.+ Sihoni inali mfumu ya Aamori,+ ndipo iye ndiye anamenyana ndi mfumu ya Mowabu m’mbuyomo, n’kulanda dziko lonse limene linali m’manja mwake mpaka kuchigwa cha Arinoni.+ 27 N’chifukwa chake olakatula ndakatulo zonyoza anali kunena kuti:
“Bwerani ku Hesiboni.
Mzinda wa Sihoni umangidwe n’kukhala wolimba.
28 Pakuti moto watuluka ku Hesiboni,+ lawi lamoto latuluka m’tauni ya Sihoni.
Lanyeketsa Ari+ mzinda wa ku Mowabu, lanyeketsa eni ake a malo okwezeka a ku Arinoni.
29 Tsoka iwe Mowabu! Ndithu mudzafafanizika, inu anthu a Kemosi!+
Ndithudi, iye adzapangitsa ana ake aamuna kukhala othawa kwawo, ndipo adzapereka ana ake aakazi mu ukapolo kwa Sihoni, mfumu ya Aamori.
30 Choncho tiyeni tiwalase.
Ndithu Hesiboni adzafafanizika mpaka ku Diboni,+
Amayi adzaphedwa mpaka ku Nofa, amuna mpaka ku Medeba.”+
31 Tsopano Aisiraeli anayamba kukhala m’dziko la Aamori.+ 32 Pamenepo Mose anatumiza anthu ena kuti akazonde mzinda wa Yazeri.+ Atatero, Aisiraeliwo analanda midzi yozungulira mzindawo, n’kupitikitsa Aamori omwe anali kukhalamo.+ 33 Pambuyo pake, anatembenuka ndi kulowera njira ya ku Basana.+ Pamenepo, Ogi+ mfumu ya Basana inatuluka pamodzi ndi anthu ake onse kukamenyana nawo pankhondo ya ku Edirei.+ 34 Tsopano Yehova analankhula ndi Mose kuti: “Usamuope ameneyu,+ chifukwa ndim’pereka ndithu m’manja mwako. Ndim’pereka pamodzi ndi anthu ake onse ndi dziko lake.+ Umuchite zimene unachitira Sihoni mfumu ya Aamori, amene anali kukhala m’Hesiboni.”+ 35 Choncho Aisiraeliwo anapha iyeyo, ana ake ndi anthu ake onse, moti sipanatsale ndi mmodzi yemwe wopulumuka,+ ndipo analanda dziko lake.+