31 Ndiyeno anauza Aroni ndi ana ake kuti: “Wiritsani+ nyamayo pakhomo la chihema chokumanako, ndipo muidyerenso pomwepo+ pamodzi ndi mkate umene uli m’dengu logwiritsidwa ntchito polonga anthu unsembe, monga mmene anandilamulira, kuti, ‘Aroni ndi ana ake adye zimenezi.’