23 Aroni anatenga Eliseba, mwana wamkazi wa Aminadabu, mlongo wake wa Naasoni,+ kukhala mkazi wake. Ndipo Eliseba anam’berekera Nadabu, Abihu, Eleazara ndi Itamara.+
16 “Eleazara mwana wa wansembe Aroni, aziyang’anira+ mafuta+ a nyale, zofukiza zonunkhira,+ nsembe yanthawi zonse yambewu,+ ndi mafuta odzozera.+ Aziyang’aniranso chihema chonse chopatulika ndi zonse za mmenemo, ndiwo malo oyerawo ndi ziwiya zake.”