53 Alevi azimanga mahema awo mozungulira chihema cha Umboni kuti mkwiyo+ wa Mulungu usawayakire ana a Isiraeli. Aleviwo azitumikira pachihema cha Umbonicho.”+
32 Ana a Leviwa analinso ndi ntchito yolondera+ chihema chokumanako, malo oyera,+ ndiponso yolondera abale awo, ana a Aroni, pa utumiki wa panyumba ya Yehova.+
11 Kenako Aleviwo adzakhala atumiki m’malo anga opatulika. Adzakhala ndi maudindo oyang’anira zipata za Nyumba ino ndipo adzakhala atumiki a pa Nyumbayi.+ Iwo azidzapha nyama za nsembe yopsereza yathunthu ndi nsembe zina za anthu+ ndipo adzaimirira pamaso pa anthuwo ndi kuwatumikira.+