15 Komabe, m’kachizirezire ka m’bandakucha, angelowo anayamba kum’fulumiza Loti, kuti: “Fulumira! Tenga mkazi wako ndi ana ako aakazi awiriwa,+ kuti musawonongedwere limodzi ndi mzindawu chifukwa cha kulakwa kwake.”+
4 Ndipo ndinamva mawu ena kumwamba, akuti: “Tulukani mwa iye anthu anga,+ ngati simukufuna kugawana naye machimo ake,+ ndiponso ngati simukufuna kulandira nawo ina ya miliri yake.