7 Kunena za ine, pamene ndinali kuchokera ku Padani,+ mayi ako Rakele anandifera+ panjira m’dziko la Kanani, patatsala mtunda ndithu kuti tifike ku Efurata. Zitatero, ndinawaika m’manda panjira yopita ku Efurata,+ kapena kuti Betelehemu.”+
12 Tsopano Davide anali mwana wamwamuna wa Jese, Mwefurata+ wina wa ku Betelehemu, ku Yuda. Jese anali ndi ana aamuna 8+ ndipo m’masiku a Sauli iye anali atakalamba kale.