7 Inunso amuna,+ pitirizani kukhala ndi akazi anu mowadziwa bwino,+ ndi kuwapatsa ulemu+ monga chiwiya chosalimba, kuti mapemphero anu asatsekerezedwe,+ pakuti mudzalandira nawo limodzi moyo+ umene Mulungu adzakupatseni chifukwa cha kukoma mtima kwake kwakukulu.