19 Wansembe atenge mwendo wakutsogolo wa nkhosa yamphongo umene wawiritsidwa.+ Atengenso m’dengumo mkate woboola pakati wopanda chofufumitsa, ndi kamkate kopyapyala kopanda chofufumitsa.+ Zinthuzi aziike m’manja mwa Mnaziriyo atameta chizindikiro cha unaziri wake.