8 Asa anakhala ndi gulu lankhondo lonyamula zishango zazikulu+ ndi mikondo ing’onoing’ono,+ la asilikali 300,000 a fuko la Yuda.+ Analinso ndi asilikali onyamula zishango zazing’ono+ ndi odziwa kupinda uta okwanira 280,000+ a fuko la Benjamini. Onsewa anali amuna amphamvu ndi olimba mtima.