19 Nyumba yopatulika ya pakachisi wa Mulungu imene ili kumwamba+ inatsegulidwa, ndipo likasa+ la pangano lake linaonekera m’nyumba yake yopatulika+ ya pakachisi. Pamenepo kunachitika mphezi, kunamveka mawu, kunagunda mabingu, kunachita chivomezi, ndipo kunagwa matalala ambiri zedi.