Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yesaya 30:33
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 33 Malo otchedwa Tofeti*+ owonongerako Asuri akonzedwa kale. Malowo akonzedweranso mfumu yawo.+ Malo amene iye wakonzawo ndi ozama ndipo kuli moto waukulu ndi nkhuni zambiri. Mpweya wa Yehova ukuyatsa malowo ngati mtsinje wa sulufule.+

  • Yeremiya 7:31
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 31 Iwo amanga malo okwezeka ku Tofeti,+ m’chigwa cha mwana wa Hinomu,+ kuti azitentha ana awo aamuna ndi ana awo aakazi pamoto,+ chinthu chimene sindinawalamule kuchita ndiponso chimene sindinachiganizirepo mumtima mwanga.’+

  • Yeremiya 19:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 6 “‘Yehova wanena kuti: “Chotero taonani! Masiku akubwera pamene sadzatchulanso malowo kuti Tofeti+ ndiponso chigwa cha mwana wa Hinomu,+ koma adzawatchula kuti chigwa chopherako anthu.

  • Yeremiya 19:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Ndiyeno ukawauze kuti, ‘Yehova wa makamu wanena kuti: “Mofanana ndi zimenezi, ndidzaswa anthu awa ndi mzinda uwu ngati mmene munthu amaswera botolo lopangidwa ndi woumba mbiya moti sangathe kulikonzanso.+ Ndipo adzaika maliro ku Tofeti+ mpaka sipadzapezekanso malo oika maliro kumeneko.”’+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena