64 “Yehova adzakumwazani mwa anthu a mitundu yonse kuchokera kumalekezero ena a dziko mpaka kumalekezero enanso a dziko.+ Kumeneko mukatumikira milungu ina imene inuyo kapena makolo anu simunaidziwe, milungu yamtengo ndi milungu yamwala.+
23 mpaka Yehova anachotsa Isiraeli pamaso pake+ monga momwe ananenera kudzera mwa atumiki ake onse, aneneri.+ Choncho Isiraeli anachoka m’dziko lake n’kupita ku Asuri, ndipo ali komweko mpaka lero.+