6 Ezara ameneyu ananyamuka n’kuchoka ku Babulo. Iye anali katswiri wodziwa kukopera+ chilamulo cha Mose,+ chimene Yehova Mulungu wa Isiraeli anapereka. Chotero mfumu inamupatsa zopempha zake zonse chifukwa dzanja la Yehova Mulungu wake linali pa iye.+
28 Iye wandisonyeza kukoma mtima kosatha+ pamaso pa mfumu, pamaso pa aphungu ake,+ ndi pamaso pa akalonga onse amphamvu a mfumu. Ineyo ndinadzilimbitsa chifukwa dzanja+ la Yehova Mulungu wanga linali pa ine, ndipo ndinasonkhanitsa atsogoleri a Aisiraeli kuti apite nane limodzi.