12 Pa zikondwerero zawo amaimbapo azeze, zoimbira za zingwe, maseche, ndi zitoliro ndipo amamwapo vinyo.+ Koma sayang’ana ntchito ya Yehova, ndipo ntchito ya manja ake saiona.+
13 Komatu anthuwo adzakondwera ndi kusangalala. Adzapha ng’ombe ndi nkhosa. Adzadya nyama ndi kumwa vinyo.+ Iwo adzati, ‘Tiyeni tidye ndi kumwa, pakuti mawa tifa.’”+