3 Iye anali ndi ziweto+ izi: Nkhosa 7,000, ngamila 3,000, ng’ombe 1,000 zomwe zinali kugwira ntchito zili ziwiriziwiri, ndi abulu aakazi 500. Analinso ndi antchito ochuluka zedi, ndipo iye anali munthu wolemekezeka kwambiri pa anthu onse a Kum’mawa.+