13 Pakuti iye wanena kuti, ‘Ndi mphamvu za dzanja langa ndiponso ndi nzeru zanga, ndidzachitapo kanthu+ chifukwa ndine wodziwa zinthu. Ndidzachotsa malire a mitundu ya anthu,+ ndipo zinthu zimene anasunga ndidzazilanda.+ Monga munthu wamphamvu, ndidzagwetsa anthu okhala mmenemo.+