20 Mtambowo unaima pakati pa Aiguputo ndi Aisiraeli.+ Mbali imodzi unali kuchititsa mdima, ndipo mbali ina unali kuwaunikira usiku.+ Ndipo gulu la Aiguputo silinayandikire gulu la Aisiraeli usiku wonse.
24 Ndiyeno pa nthawi ya ulonda wam’mawa,* Yehova ali mumtambo ndi moto woima njo ngati chipilala,+ anayang’ana gulu la Aiguputo, ndipo anachititsa Aiguputowo kusokonezeka.+