14 Iyo inayamba kulankhula kwa anthuwo motsatira malangizo amene achinyamata aja+ anaipatsa. Inati: “Bambo anga anakusenzetsani goli lolemera, koma ine ndidzawonjezera goli lanulo. Bambo anga anakukwapulani ndi zikwapu, koma ine ndidzakukwapulani ndi zikoti zaminga.”+