15 “M’malo mokhala wosiyidwa mpaka kalekale ndi wodedwa, popanda aliyense wodutsa mwa iwe,+ ine ndidzakuika monga chinthu chonyaditsa mpaka kalekale, ndiponso chinthu chokondweretsa ku mibadwomibadwo.+
11 Iye anandiuzanso kuti: “Iwe mwana wa munthu, mafupawa akuimira nyumba yonse ya Isiraeli.+ Iwo akunena kuti, ‘Mafupa athu auma ndipo tilibenso chiyembekezo chilichonse.+ Atilekanitsa ndi anzathu ndipo tili kwatokhatokha.’