-
1 Mafumu 18:26Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
26 Choncho anatenga ng’ombe yaing’ono yamphongo imene Eliya anawapatsa, n’kuikonza. Kenako anayamba kuitana dzina la Baala kuyambira m’mawa mpaka masana. Ankaitana kuti: “Inu a Baala, tiyankheni!” Koma sipanamveke mawu alionse,+ ndipo palibe anayankha.+ Iwo anapitiriza kudumphadumpha ngati akuvina, kuzungulira guwa lansembe limene anamanga.
-
-
Yeremiya 50:2Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
2 “Nenani ndi kulengeza zimene zachitika kwa anthu a mitundu ina.+ Imikani mtengo wachizindikiro+ ndipo lengezani zimenezi. Musabise kalikonse amuna inu. Nenani kuti, ‘Babulo walandidwa.+ Beli wachititsidwa manyazi.+ Merodake wachita mantha. Mafano a Babulo achita manyazi.+ Mafano ake onyansawo* achita mantha.’
-