13 Mmisiri wosema mtengo watambasula chingwe choyezera. Waulemba ndi choko chofiira. Wausema ndi sompho ndipo waulemberera ndi chida cholembera mizere yozungulira. Pang’ono ndi pang’ono waupanga kuti uzioneka ngati munthu,+ ngati kukongola kwa anthu, kuti uzikhala m’nyumba.+