14 Koma Isiraeli anatambasula dzanja lake lamanja n’kuliika pamutu pa Efuraimu,+ ngakhale kuti ndiye anali wamng’ono.+ Anatambasulanso dzanja lake lamanzere n’kuliika pamutu pa Manase.+ Anasemphanitsa dala choncho manja ake chifukwa Manase ndiye anali mwana woyamba.+