40Awa ndi mawu amene Yehova anauza Yeremiya, pamene Nebuzaradani+ mkulu wa asilikali olondera mfumu anamumasula ku Rama.+ Yeremiya anali womangidwa maunyolo a m’manja pamene Nebuzaradani anamutenga pakati pa anthu a ku Yerusalemu ndi a ku Yuda amene anali kupita ku ukapolo ku Babulo.+
12 Ndiyeno m’mwezi wachisanu, pa tsiku la 10 la mweziwo, m’chaka cha 19 cha ulamuliro wa Mfumu Nebukadirezara+ ya Babulo, Nebuzaradani+ mkulu wa asilikali olondera mfumu, amene anali kutumikira mfumu ya Babulo, anabwera ku Yerusalemu.