7 Yerusalemu anakumbukira zinthu zake zonse zabwino+ zimene anali nazo kuyambira kalekale.
Anazikumbukira m’masiku a masautso ake ndi a anthu ake osowa pokhala.
Anthu ake atagwidwa ndi adani, pamene iye analibe munthu womuthandiza,+
Adani akewo anamuona, ndipo anamuseka+ chifukwa chakuti wagwa.