Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Levitiko 26:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 6 Ndidzakupatsani mtendere m’dzikolo,+ moti mudzagona pansi popanda wokuopsani.+ M’dziko lanu simudzapezeka zilombo zoopsa zakutchire,+ ndipo simudzadutsa lupanga.+

  • Yesaya 11:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 6 Mmbulu udzakhala pamodzi ndi mwana wa nkhosa wamphongo kwa kanthawi,+ ndipo kambuku* adzagona pansi ndi mwana wa mbuzi. Mwana wa ng’ombe, mkango wamphamvu+ ndi nyama yodyetsedwa bwino zidzakhala pamodzi,+ ndipo kamnyamata kakang’ono kadzakhala mtsogoleri wawo.

  • Yesaya 35:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Kumeneko sikudzakhala mkango ndipo nyama zolusa zakutchire sizidzafikako.+ Nyama zotere sizidzapezekako.+ Anthu ogulidwanso adzayenda mumsewuwo.+

  • Yesaya 65:25
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 25 “Mmbulu+ ndi mwana wa nkhosa zidzadyera pamodzi.+ Mkango udzadya udzu ngati ng’ombe yamphongo,+ ndipo njoka izidzadya fumbi.+ Zimenezi sizidzapweteka aliyense+ kapena kuwononga chilichonse m’phiri langa lonse loyera,”+ watero Yehova.

  • Hoseya 2:18
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 18 Pa tsiku limenelo ndidzachita pangano ndi chilombo chakuthengo,+ cholengedwa chouluka m’mlengalenga ndi cholengedwa chokwawa panthaka, kuti ndithandize anthu anga. Ndidzathyola uta ndi lupanga ndipo ndidzathetsa nkhondo padziko.+ Pamenepo ndidzawachititsa kukhala mwabata.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena