-
Ezekieli 40:9Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
9 Anayeza khonde la kanyumba ka pachipata n’kupeza kuti linali mikono 8. Zipilala zake zam’mbali zinali mikono iwiri. Khonde la kanyumbako linali loyang’ana kubwalo lakunja.
-
-
Ezekieli 46:2Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
2 Mtsogoleri wa anthu azilowa kuchokera panja n’kufika pakhonde la kanyumba ka pachipata+ ndipo aziima pafupi ndi felemu la chipatacho.+ Ndiyeno ansembe azimuperekera nsembe yopsereza yathunthu ndi nsembe zake zachiyanjano. Mtsogoleriyo azigwada ndi kuwerama pakhomo la kanyumba ka pachipata,+ kenako azituluka koma chipatacho chisamatsekedwe kufikira madzulo.
-