-
1 Samueli 7:3Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
3 Zitatero, Samueli anauza nyumba yonse ya Isiraeli kuti: “Ngati mukubwereradi kwa Yehova+ ndi mtima wanu wonse, chotsani milungu yachilendo pakati panu.+ Muchotsenso zifaniziro za Asitoreti,+ ndi kulunjikitsa mitima yanu kwa Yehova mosayang’ananso kwina,+ ndi kutumikira iye yekha. Mukatero, adzakupulumutsani m’manja mwa Afilisiti.”+
-
-
Ezekieli 33:12Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
12 “Iwe mwana wa munthu, uza anthu a mtundu wako kuti, ‘Munthu wolungama akapanduka, chilungamo chake sichidzamupulumutsa pa tsiku la kupanduka kwake.+ Koma munthu woipa akabwerera n’kusiya zoipa zakezo, sadzafa chifukwa cha zoipazo pa tsiku limene adzabwerere n’kuzisiya.+ Komanso munthu wolungama sadzakhalabe ndi moyo chifukwa cha chilungamo chake pa tsiku limene adzachimwe.+
-