Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ekisodo 20:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 “Pokumbukira kuti muyenera kusunga tsiku la sabata ndi kuliona kukhala lopatulika,+

  • Levitiko 23:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 “‘Muzigwira ntchito masiku 6, koma tsiku la 7 likhale sabata lopuma pa ntchito zanu zonse.+ Limeneli ndi tsiku la msonkhano wopatulika. Musagwire ntchito iliyonse chifukwa limeneli ndi sabata la Yehova kulikonse kumene mungakhale.+

  • Levitiko 23:24
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 “Lankhula ndi ana a Isiraeli, ndipo uwauze kuti, ‘M’mwezi wa 7,+ pa tsiku loyamba m’mweziwo, muzipuma pa ntchito zanu zonse. Limeneli ndi tsiku la chikumbutso, tsiku loliza lipenga,+ tsiku la msonkhano wopatulika.+

  • Levitiko 23:32
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 32 Ili ndi sabata lopuma pa ntchito zanu zonse,+ ndipo muzidzisautsa+ madzulo pa tsiku la 9 m’mweziwo. Muzisunga sabata kuyambira madzulo kufikira madzulo tsiku lotsatira.”

  • Levitiko 25:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 Koma m’chaka cha 7 dzikolo lizisunga sabata lopuma pa zonse,+ sabata la Yehova. Musalime minda yanu, ndipo musatengulire mitengo yanu ya mpesa.

  • Levitiko 25:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Chaka cha 50 ndi Chaka cha Ufulu kwa inu.+ Musalime minda yanu kapena kukolola mbewu zomera zokha, kapenanso kukolola mphesa za m’mitengo yosadulirayo.+

  • Deuteronomo 5:12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 “‘Posunga tsiku la sabata ndi kuliona kukhala lopatulika, mmene Yehova Mulungu wako anakulamulira,+

  • Nehemiya 9:14
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 14 Munawaphunzitsa za sabata lanu lopatulika.+ Munawapatsa malangizo, mfundo ndi chilamulo kudzera mwa Mose mtumiki wanu.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena