10 M’chaka chachitatu cha ulamuliro wa Koresi+ mfumu ya Perisiya, panali nkhani imene Danieli anauzidwa. Danieli ameneyu anali kutchedwa Belitesazara.+ Nkhani imene anauzidwayo inali yoona ndipo inali yokhudza nkhondo yaikulu.+ Danieli anamvetsa nkhani imeneyi ndiponso zinthu zimene anaona.+