2 Mafumu 2:11 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 11 Pamene anali kuyenda n’kumalankhulana, anangoona galeta*+ lankhondo lowala ngati moto ndi mahatchi* owala ngati moto. Galeta ndi mahatchiwo zinadutsa pakati pawo n’kuwalekanitsa, ndipo Eliya anatengedwa mumphepo yamkuntho n’kukwera kumwamba.+ Mateyu 17:3 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 3 Kenako Mose ndi Eliya anaonekera kwa iwo akukambirana ndi Yesu.+ Maliko 9:4 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 4 Komanso, Eliya ndi Mose anaonekera kwa iwo, ndipo anali kukambirana ndi Yesu.+
11 Pamene anali kuyenda n’kumalankhulana, anangoona galeta*+ lankhondo lowala ngati moto ndi mahatchi* owala ngati moto. Galeta ndi mahatchiwo zinadutsa pakati pawo n’kuwalekanitsa, ndipo Eliya anatengedwa mumphepo yamkuntho n’kukwera kumwamba.+