6 Tsopano m’masiku amenewo, pamene ophunzirawo anali kuchulukirachulukira, Ayuda olankhula Chigiriki+ anayamba kudandaula za Ayuda olankhula Chiheberi. Chifukwa chakuti akazi amasiye achigiriki anali kunyalanyazidwa pa kagawidwe ka chakudya cha tsiku ndi tsiku.+