37 Tsopano pa tsiku lomaliza, tsiku lalikulu la chikondwererocho,+ Yesu anaimirira ndi kufuula kuti: “Ngati wina akumva ludzu,+ abwere kwa ine adzamwe madzi.
17 chifukwa Mwanawankhosa,+ amene ali pambali pa mpando wachifumu, adzawaweta+ ndi kuwatsogolera ku akasupe a madzi+ a moyo. Ndipo Mulungu adzapukuta misozi yonse m’maso mwawo.”+
6 Anandiuzanso kuti: “Zakwaniritsidwa! Ine ndine Alefa ndi Omega, chiyambi ndi mapeto.+ Aliyense womva ludzu, ndidzamupatsa madzi a m’kasupe wa moyo kwaulere.+