Yona
2 Tsopano Yona anapemphera kwa Yehova Mulungu wake, ali m’mimba mwa chinsombacho,+ 2 kuti:
“Pamene ndinali m’masautso ndinaitana Yehova,+ ndipo anandiyankha.+
Ndinafuula kupempha thandizo ndili m’Manda* akuya.+
Ndipo inu munamva mawu anga.+
3 Pamene munandiponya m’malo ozama, pansi penipeni pa nyanja yakuya,+
Madzi amphamvu anandimiza.
Mafunde anu amphamvu anadutsa pamwamba panga.+
6 Ndinatsikira m’tsinde mwenimweni mwa mapiri.
Zotsekera za dziko lapansi zinanditsekereza kuti ndikhale komweko mpaka kalekale.*
Koma inu Yehova Mulungu wanga, munanditulutsa m’dzenje ndili wamoyo.+
7 Pamene ndinalefuka kwambiri,+ ndinakumbukira Yehova.+
Ndipo pemphero langa linafika kwa inu, m’kachisi wanu woyera.+
8 Anthu okhulupirira mafano, amaleka kusonyeza kukoma mtima kwawo kosatha.+
9 Koma ine, ndidzakutamandani ndi kupereka nsembe kwa inu.+
Zimene ndalonjeza ndidzazikwaniritsa.+ Chipulumutso chimachokera kwa Yehova.”+
10 Kenako Yehova analamula chinsombacho, ndipo chinalavula Yona kumtunda.+