10 Koma Yakobo anati: “Ayi chonde, musatero. Ngati mwandikomeradi mtima, landirani mphatso yangayi, chifukwa ndabweretsa mphatsoyi kuti ndidzaone nkhope yanu, ndipo ndaionadi. Zili ngati ndaona nkhope ya Mulungu, chifukwa mwandilandira ndi manja awiri.+